Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Akolose 1:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. pakuti mwa iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yacifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa iye ndi kwa iye.

17. Ndipo iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa iye.

18. Ndipo iye ali mutu wa thupi, Eklesiayo; ndiye ciyambi, wobadwa woyamba woturuka mwa akufa; kuti akakhale iye mwa zonse woyambayamba.

19. Pakuti kunamkomera Atate kuti mwa iye cidzalo conse cikhalire,

Werengani mutu wathunthu Akolose 1