Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 9:26-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. cikadatero, kukadamuyenera kumva zowawa kawiri kawiri kuyambira kuzika kwa dziko lapansi; kama tsopano 7 kamodzi pa citsirizo ca nthawizo waonekera kucotsa ucimo mwa nsembe ya iye yekha.

27. Ndipo popeza 8 kwaikikatu kwa anthu kufa kamodzi, ndipo 9 atafa, ciweruziro;

28. kotero 10 Kristunso ataperekedwa nsembe kamodzi kukasenza macimo a ambiri, 11 adzaonekera pa nthawi yaciwiri, wopanda ucimo, kwa iwo amene amlindirira, kufikira cipulumutso.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 9