Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 9:18-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. momwemo coyambaconso sicinakonzeka copanda mwazi.

19. Pakuti pamene Mose adalankhulira anthu once lamulo liri lonse monga mwa cilamulo, anatenga mwazi wa ana a ng'ombe ndi mbuzi, pamodzi ndi madzi ndi ubweya wofiira ndi hisope, nawaza buku lomwe, ndi anthu onse,

20. nati, 1 Uwu ndi mwazi wa cipangano Mulungu adakulamulirani.

21. Ndiponso cihema ndi zotengera zonse za utumikiro anaziwaza momwemo ndi mwaziwo.

22. Ndipo monga mwa cilamulo zitsala zinthu pang'ono zosayeretsedwa ndi mwazi, ndipo 2 wopanda kukhetsa mwazi kulibe kumasuka.

23. Pomwepo padafunika kuti 3 zifaniziro za zinthu za m'Mwamba ziyeretsedwe ndi izi; koma zam'mwamba zeni zeni ziyeretsedwe ndi nsembe zoposa izi.

24. Pakuti 4 Kristu sanalowa m'malo opatulika omangika ndi manja, akutsanza oonawo; komatu m'Mwamba momwe, 5 kuonekera tsopano pamaso pa Mulungu cifukwa ca ife;

25. kosati kuti adzipereke yekha kawiri kawiri; 6 monga mkulu wa ansembe alowa m'malo opatulika caka ndi caka ndi mwazi wosati wace;

26. cikadatero, kukadamuyenera kumva zowawa kawiri kawiri kuyambira kuzika kwa dziko lapansi; kama tsopano 7 kamodzi pa citsirizo ca nthawizo waonekera kucotsa ucimo mwa nsembe ya iye yekha.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 9