Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 7:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo monga momwe sikudacitika kopanda lumbiro;

21. (pakuti iwotu anayesedwa ansembe kopanda lumbiro; koma iye ndi lumbiro mwa iye emeoe ananena kwa iye,Walumbira Ambuye ndipo sadzalapa,Iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha).

22. Momwemonso Yesu wakhala Nkhoswe ya pangano loposa.

23. Ndipo iwo ndiwo ambiri anakhala ansembe, popeza imfa idawaletsa asakhalebe;

24. koma iye cifukwa kuti akhala iye nthawi yosatha ali nao unsembe wosasinthika,

25. kucokera komwekoakhoza kupulumutsa konse konse iwo akuyandikira kwa Mulungu mwa iye, popeza ali nao moyo wace cikhalire wa kuwapembedzera iwo.

26. Pakuti mkulu wa ansembe wotere anatiyenera ife, woyera mtima, wopanda coipa, wosadetsedwa, wosiyana ndi ocimwa, wakukhala wopitirira miyamba;

27. amene alibe cifukwa ca kupereka nsembe tsiku ndi tsiku monga akulu a ansembe, yoyambira cifukwa ca zoipa za iwo eni, yinayi cifukwa ca zoipa za anthu; pakuti ici anacita kamodzi, kwatha, podzipereka yekha.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 7