Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 6:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. nalawa mau okoma a Mulungu, ndi mphamvu ya nthawi irinkudza,

6. koma anagwa m'cisokero; popeza adzipaeikiranso okha Mwana wa Mulungu, namcititsa manyazi poyera.

7. Pakuti nthaka imene idamwa mvula iigwera kawiri kawiri, nipatsa therere loyenera iwo amene adailimira, ilandira dalitso locokera kwa Mulungu:

8. koma ikabala minga ndi mitungwi, itayika; nitsala pang'ono ikadatembereredwa; citsiriziro cace ndico kutenthedwa.

9. Koma, okondedwa, takopeka mtima kuti za inu ziri zoposa ndi zophatikana cipulumutso, tingakhale titero pakulankhula;

10. pakuti Mulungu sali wosalungama kuti adzaiwala nchito yanu, ndi cikondico mudacionetsera ku dzina lace, umo mudatumikira oyera mtima ndi kuwatumikirabe.

11. Koma tikhumba kuti yense wa inu aonetsere cangu comweci colinga ku ciyembekezo cokwanira kufikira citsiriziro;

12. kuti musakhale aulesi, koma akuwatsanza iwo amene alikulowa malonjezano mwa cikhulupiriro ndi kuleza mtima.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 6