Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 6:15-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo potero atapirira analandira lonjezanolo.

16. Pakuti anthu amalumbira pa wamkulu; ndipo m'citsutsano cao ciri conse lumbiro litsiriza kutsimikiza.

17. Momwemo Mulungu, pofuna kuonetsera mocurukira kwa olowa a lonjezano kuti cifuniro cace sicisinthika, analowa pakati ndi lumbiro;

18. kuti mwa zinthu ziwiri zosasinthika, m'mene Mulungu sakhoza kunama, tikakhale naco coticenjeza colimba, ife amene tidathawira kucigwira ciyembekezo coikika pamaso pathu;

19. cimene tiri naco ngati nangula wa moyo, cokhazikika ndi colimbanso, ndi cakulowa m'katikati mwa cophimba;

20. m'mene Yesu mtsogoleri analowamo cifukwa ca ife, atakhala mkulu wa ansembe nthawi yosatha monga mwa dongosolo la Melikizedeke.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 6