Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 6:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwa ici, polekana nao mau a ciyambidwe ca Kristu, tipitirire kutsata ukulu msinkhu; osaikanso maziko a kutembenuka mtima kusiyana nazo nchito zakufa, ndi a cikhulupiriro ca pa Mulungu,

2. a ciphunzitso ca ubatizo, a kuika manja, a kuuka kwa akufa, ndi a ciweruziro cosatha.

3. Ndipo ici tidzacita, akatilola Mulungu.

4. Pakuti sikutheka kuwakonzanso, atembenuke mtima, iwo amene anaunikidwa pa nthawi yace, nalawa mphatso ya Kumwamba, nakhala olandirana naye Mzimu Woyera,

5. nalawa mau okoma a Mulungu, ndi mphamvu ya nthawi irinkudza,

Werengani mutu wathunthu Ahebri 6