Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 6:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mwa ici, polekana nao mau a ciyambidwe ca Kristu, tipitirire kutsata ukulu msinkhu; osaikanso maziko a kutembenuka mtima kusiyana nazo nchito zakufa, ndi a cikhulupiriro ca pa Mulungu,

2. a ciphunzitso ca ubatizo, a kuika manja, a kuuka kwa akufa, ndi a ciweruziro cosatha.

3. Ndipo ici tidzacita, akatilola Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 6