Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 5:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. angakhale anali Mwana, anaphunzira kumvera ndi izi adamva kuwawa nazo;

9. ndipo pamene anakonzeka wamphumphu anakhala kwa onse akumvera iye cifukwa ca cipulumutso cosatha;

10. wochedwa ndi Mulungu mkulu wa ansembe monga mwa dongosolo la Melikizedeke.

11. Za iye tirinao mau ambiri kuwanena, ndiotilaka powatanthauzira, popeza mwagontha m'makutu.

12. Pakuti mungakhale mwayenera kukhala aphunzitsi cifukwa ca nyengoyi, muli nako kusowanso kuti wina aphunzitse inu zoyamba za ciyambidwe ca maneno a Mulungu; ndipo mukhala onga ofuna mkaka, osati cakudya cotafuna.

13. Pakuti yense wakudya mkaka alibe cizolowezi ca mau a cilungamo; pakuti ali khanda.

14. Koma cakudya cotafuna ciri ca anthu akulu misinkhu, amene mwa kucita nazo anazoloweretsa zizindikiritso zao kusiyanitsa cabwino ndi coipa.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 5