Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 2:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndiponso,Ndidzamtama Iye.Ndiponso,Taonani, Ine ndi ana amene Mulungu anandipatsa,

14. Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;

15. nakamasule iwo onse amene, cifukwa ca kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.

16. Pakuti ndithu salandira angelo, koma alandira mbeu ya Abrahamu.

17. Potero kudamuyenera kufanizidwa ndi abale m'zonse, kuti akadzakhala mkulu wa ansembe wadfundo ndi wokhulupirika m'zinthu zakwa Mulungu, kuti apereke dipo la zoipa za anthu.

18. Pakuti popeza adamva zowawa, poyesedwa yekha, akhoza kuthandiza iwo amene ayesedwa.

Werengani mutu wathunthu Ahebri 2