Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ahebri 1:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mwakonda cilungamo, ndi kudana naco coipa;Mwa ici Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wakudzozaniNdi mafuta a cikondwerero ceni ceni koposa anzanu.

10. Ndipo,Inu, Ambuye, paciyambipo munaika maziko ace a dziko,Ndipo miyamba iri nchito ya manja anu;

11. Iyo idzatayika; komatu mukhalitsa;Ndipo iyo yonse idzasuka mongamaraya;

12. Ndi monga copfunda mudzaipindaMonga maraya, ndipo idzasanduka;Koma Inu ndinu yemweyo,Ndipo zaka zanu sizidzatha.

13. Koma za mngelo uti anati nthawi iri yonse,Khala pa dzanja lamanja langa,Kufikira ndikaika adani ako mpando wa ku mapazi ako?

14. Kodi siiri yonse mizimu yotumikira, yotumidwa kuti itumikire iwo amene adzalowa cipulumutso?

Werengani mutu wathunthu Ahebri 1