Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 6:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pakuti ngati wina ayesa ali kanthu pokhala ali cabe, adzinyenga yekha.

4. Koma yense ayesere nchito yace ya iye yekha, ndipo pamenepo adzakhala nako kudzitamandira cifukwa ca iye yekha, si cifukwa ca wina,

5. Pakuti yense adzasenza katundu wace wa iye mwini.

6. Koma iye amene aphunzira mau, ayenera kucereza womphunzitsayo m'zonse zabwino.

7. Musanyengedwe; Mulungu sanyozeka; pakuti cimene munthu acifesa, cimenenso adzacituta.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 6