Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 6:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Koma kudzitamandira ine konse konse, iai, koma mu mtanda wa Ambuye wathu Yesu Kristu, amene mwa iye dziko lapansi lapacikidwira ine, ndi ine ndapacikidwira dziko lapansi.

15. Pakuti mdulidwe ulibe kanthu, kusadulidwakulibe kanthunso, komatu wolengedwa watsopano.

16. Ndipo onse amene atsatsa cilangizo ici, mtendere ndi cifundo zikhale pa iwo, ndi pa Israyeli wa Mulungu.

17. Kuyambira tsopano palibe munthu andibvute, pakuti ndiri nayo ine m'thupi mwanga mikwingwirima ya Yesu.

18. Cisomo ca Ambuye wathu Yesu Kristu cikhale ndi mzimu wanu, abale. Amen.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 6