Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 5:3-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndicitanso umboni kwa munthu yense wolola amdule, kuti ali wamangawa kucita cilamulo conse.

4. Mulibe kanthu ndi Kristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana naco cisomo.

5. Pakuti ife mwa Mzimu, kucokera m'cikhulupiriro, tilindira ciyembekezo ca cilungamo,

6. Pakuti mwa Kristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu cikhulupiriro cakucititsa mwa cikondi.

7. Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere coonadi?

8. Kukopa kumene sikucokera kwa iye anakuitanani.

9. Cotupitsa pang'ono citupitsa mtanda wonse.

10. Ine ndikhulupirira inu mwa Ambuye, kuti simudzakhala nao mtima wina; koma iye wakubvuta inu, angakhale ali yani, adzasenza citsutso cace.

11. Koma ine, abale, ngati ndilalikiransoindulidwe, ndizunzikanso bwanji? Pamenepo cikhumudwitso ca mtanda cidatha.

12. Mwenzi atadzidula, iwo akugwedezetsani inu.

13. Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; cokhaco musacite nao ufulu wanu cothandizira thupi, komatu mwa cikondi citiranani ukapolo.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 5