Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 5:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazicite.

18. Ngati Mzimu akutsogolerani, simuli omvera lamulo.

19. Ndipo nchito za thupi zionekera, ndizo dama, codetsa, kukhumba zonyansa, kupembedza mafano,

20. nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru,

21. kuledzera, mcezo, ndi zina zotere; zimene ndikucenjezani nazo, monga ndacita, kuti iwo akucitacita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu.

22. Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza mtima, cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro,

23. cifatso, ciletso; pokana zimenezi palibe lamulo.

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 5