Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 4:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Kotero kuti sulinso kapolo, koma mwana; koma ngati mwana, wolowa nyumbanso mwa Mulungu.

8. Komatu pajapo, posadziwa Mulungu inu, munacitira ukapolo iyo yosakhalamilungu m'cibadwidwe cao;

9. koma tsopano, podziwa Mulungu inu, koma makamaka podziwika ndi Mulungu, mubwereranso bwanji kutsata miyambo yofoka ndi yaumphawi, imene mufuna kubwerezanso kuicitira ukapolo?

10. Musunga masiku, ndi miyezi, ndi nyengo, ndi zaka.

11. Ndiopera inu, kuti kapena odadzibvutitsa ndi inu cabe.

12. Abale, ndikupemphani, khalani monga ine, pakuti inenso ndiri mongainu. Simunandicitira coipa ine;

13. koma mudziwa kuti m'kufoka kwa thupi ndinakulalikirani Uthenga Wabwino poyamba:

14. ndipo cija ca m'thupi langa cakukuyesani inu simunacipeputsa, kapena sicinakunyansirani, komatu munandilandira ine monga mngelo wa Mulungu, monga Kristu Yesu mwini.

15. Pamenepo thamo lanu liri kuti? Pakuti ndikucitirani inu umboni, kuti, kukadatheka, mukadakolowola maso anu ndi kundipatsa ine.

16. Kotero kodi ndasanduka mdani wanu, pakukunenerani zoona?

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 4