Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Agalatiya 2:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo popita zaka khumi ndi zinai ndinakweranso kunka ku Yerusalemu pamodzi ndi Bamaba, ndinamtenganso Tito andiperekeze.

2. Koma ndinakwera kunkako mobvumbulutsa; ndipo ndinawauza Uthenga Wabwino umene ndiulalikira kwa amitundu; koma m'tseri kwa iwo omveka, kuti kapena ndingathamange, kapena ndikadathamanga cabe.

3. Komatu ngakhale Tito, amene anali ndi ine, ndiye Mhelene, sanamkakamiza adulidwe;

4. ndico cifukwa ca abale onyenga olowezedwa m'tseri, amene analowa m'tseri kudzazonda ufulu wathu umene tiri nao mwa Kristu Yesu, kuti akaticititse iukapolo.

5. Koma sitidawafumukira mowagonjera ngakhale ora limodzi; kuti coonadi ca Uthenga Wabwino cikhalebe ndi inu.

6. Koma iwo akuyesedwa ali kanthu (ngati anali otani kale, kulibe kanthu kwa ine; Mulungu salandira nkhope ya munthu) iwo omvekawo sanandionjezera ine kanthu;

7. koma pena, pakuona kuti anaikiza kwa ine Uthenga Wabwino wa kusadulidwa, monga kwa Petro Uthenga Wabwino wa mdulidwe

Werengani mutu wathunthu Agalatiya 2