Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 4:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

7. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana cidziwitso conse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu.

8. Cotsalira, abale, zinthu ziri zonse zoona, ziri zonse zolemekezeka, ziri zonse zolungama, ziri zonse zoyera, ziri zonse zokongola, ziri zonse zimveka zokoma; ngati kuli cokoma mtima cina, kapena citamando cina, zilingirireni izi.

9. Zimenenso mudaziphunzira, ndi kuzilandira, ndi kuzimva, ndi kuziona mwa ine, zomwezo citani; ndipo Mulungu wa mtendere adzakhala pamodzi ndi inu.

10. Koma ndinakondwera mwa Ambuye kwakukuru, kuti tsopano munatsitsimukanso kulingirira mtima za kwa ine, kumenekonso munalingirirako, koma munasowa pocitapo.

11. Si kuti ndinena monga mwa ciperewero, pakuti ndaphunzira ine, kuti zindikwanire ziri zonse ndiri nazo.

12. Ndadziwa ngakhale kupeputsidwa, ndadziwanso kusefukira; konseko ndi m'zinthu zonse ndalowa mwambo wakukhuta, ndiponso wakumva njala; wakusefukira, ndiponso wakusowa.

13. Ndikhoza zonse mwa iye wondipatsa mphamvuyo.

14. Koma munacita bwino kuti munayanjana nane m'cisautso canga.

15. Koma mudziwanso inu nokha, inu Afilipi, kuti m'ciyambi ca Uthenga Wabwino, pamene ndinacoka kuturuka m'Makedoniya, sunayanjana nane Mpingo umodzi wonse m'makhalidwe a copereka ndi colandira; koma inu nokha;

16. pakuti m'Tesalonikanso munanditumizira pa cosowa canga kamodzi kapena kawiri.

17. Sikunena kuti nditsata coperekaco, komatu nditsata cipatsocakucurukira ku ciwerengero canu.

18. Koma ndiri nazo zonse, ndipo ndisefukira; ndadzazidwa, popeza ndalandira kwa Epafrodito zija zidacokera kwanu, mnunkho wa pfungo labwino, nsembe yolandirika, yokondweretsa Mulungu.

19. Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa cosowa canu ciri conse monga mwa cuma cace m'ulemerero mwa Kristu Yesu.

20. Ndipo kwa Mulungu ndi Atate wathu kukhale ulemerero ku nthawi za nthawi, Amen.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 4