Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 4:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

5. Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.

6. Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

7. Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana cidziwitso conse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu.

8. Cotsalira, abale, zinthu ziri zonse zoona, ziri zonse zolemekezeka, ziri zonse zolungama, ziri zonse zoyera, ziri zonse zokongola, ziri zonse zimveka zokoma; ngati kuli cokoma mtima cina, kapena citamando cina, zilingirireni izi.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 4