Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 4:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Potero, abale anga okondedwa, olakalakidwa, ndinu cimwemwe canga ndikorona wanga, cirimikani motere mwa Ambuye, okondedwa.

2. Ndidandaulira Euodiya, ndidandaulira Suntuke, alingirire ndi mtima umodzi mwa Ambuye.

3. Inde, ndikupemphaninso, mnzanga wa m'goli woona, muthandize akazi awa amene anakangalika nane pamodzi mu Uthenga Wabwino, pamodzi ndi Klementonso, ndi otsala aja anchito anzanga, amene maina ao ali m'buku la moyo.

4. Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.

5. Kufatsa kwanu kuzindikirike ndi anthu onse. Ambuye ali pafupi.

6. Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 4