Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 2:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Koma muzindikira matsimikizidwe ace, kuti, monga mwana acitira atate wace, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino.

23. Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posacedwa m'mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani;

24. koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga.

25. Koma ndinayesa nkufunika kutuma kwa inu Epafrodito mbaleyo, ndiye wanchito mnzanga ndi msilikari mnzanga, ndiye mtumwi wanu, ndi wonditumikira pa cosowa canga;

Werengani mutu wathunthu Afilipi 2