Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 2:19-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma ndiyembekeza mwa Ambuye Yesu kuti ndidzatumiza Timoteo kwa inu msanga, kuti inenso nditonthozeke bwino pozindikira za kwa inu.

20. Pakuti ndiribe wina wa mtima womwewo, amene adza: samalira za kwa inu ndi mtima woona.

21. Pakuti onsewa atsata za iwo okha, si za Yesu Kristu.

22. Koma muzindikira matsimikizidwe ace, kuti, monga mwana acitira atate wace, anatumikira pamodzi ndi ine Uthenga Wabwino.

23. Ameneyo ndithu tsono ndiyembekeza kumtuma posacedwa m'mene ndikapenyerera za kwa ine zidzatani;

24. koma ndikhulupirira mwa Ambuye kuti ine ndekhanso ndidzadza msanga.

25. Koma ndinayesa nkufunika kutuma kwa inu Epafrodito mbaleyo, ndiye wanchito mnzanga ndi msilikari mnzanga, ndiye mtumwi wanu, ndi wonditumikira pa cosowa canga;

26. popeza anali wolakalaka inu nonse, nabvutika mtima cifukwa mudamva kuti anadwala.

27. Pakutinso anadwaladi pafupi imfa; komatu Mulungu anamcitira cifundo; koma si iye yekha, komatu inenso, kuti ndisakhale naco cisoni cionjezere-onjezere.

28. Cifukwa cace ndamtuma iye cifulumizire, kuti pakumuona mukakondwerenso, ndi inenso cindicepere cisoni.

29. Cifukwa cace mumlandire mwa Ambuye, ndi cimwemweconse; nimucitire ulemu oterewa;

30. pakuti cifukwa lea nchito ya Kristu anafikira pafupi imfa, wosasamalira moyo wace, kuti z akakwaniritse ciperewero ca utumiki wanu wa kwa ine.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 2