Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Afilipi 1:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. koma ena alalikira Kristu mocokera m'cotetana, kosati koona, akuyesa kuti adzandibukitsira cisautso m'zomangira zanga.

18. Potero nciani? Cokhaco kuti monsemo, ngati pamaso pokha, ngati m'coonadi, Kristu alalikidwa; ndipo m'menemo ndikondwera, komanso ndidzakondwera.

19. Pakuti ndidziwa kuti ici cidzandicitira ine cipulumutso, mwa pembedzero lanu ndi mwa kundipatsako kwa Mzimu wa Yesu Kristu;

20. monga mwa kulingiriritsa ndi ciyembekezo canga, kuti palibe cinthu cidzandicititsa manyazi, komatu mwa kulimbika mtima konse, monga nthawi yonse, tsopanonso Kristu adzakuzidwa m'thupi langa, kapena mwamoyo, kapena mwa imfa.

21. Pakuti kwa ine kukhala ndi moyo ndiko Kristu, ndi kufa kuli kupindula.

22. Koma ngati kukhala ndi moyo m'thupi, ndiko cipatso ca nchito yanga, sindizindikiranso cimene ndidzasankha.

Werengani mutu wathunthu Afilipi 1