Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 6:1-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ananu, mverani akukubalani mwa Ambuye, pakuti ici ncabwino.

2. Lemekeza atate wako ndi amako (ndilo lamulo loyamba lokhala nalo lonjezano),

3. kuti kukhale bwino ndi iwe, ndi kuti ukhale wa nthawi yaikuru padziko.

4. Ndipo atate inu, musakwiyitse ana anu; komatu muwalere iwo m'maleredwe ndi cilangizo ca Ambuye.

5. Akapolo inu, mverani iwo amene ali ambuye anu monga mwa thupi, ndi kuwaopa ndi kunthunthumira nao, ndi mtima wanu wosakumbukila kanthu kena, monga kwa Kristu;

6. si monga mwa ukapolo wa pamaso, monga okondweretsa anthu, komatu monga akapolo a Kristu, akucita cifuniro ca Mulungu cocokera kumtima;

7. akucita ukapolo ndi kubvomereza mtima, monga kutumikira Yesu Kristu, si anthu ai;

8. podziwa kuti cinthu cokoma ciri conse yense acicita, adzambwezera comweci Ambuye, angakhale ali kapolo kapena mfulu.

9. Ndipo, ambuye inu, muwacitire zomwezo iwowa, nimuleke kuwaopsa; podziwa kuti Ambuye wao ndi wanu ali m'Mwamba, ndipo palibe tsankhu kwa iye.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 6