Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Aefeso 2:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. ndi kuti akayanianitse awiriwa ndi Mulungu, m'thupi limodzi mwa mtandawo, atapha nao udaniwo;

17. ndipo m'mene anadza, analalikira Uthenga Wabwino wa mtendere kwa inu akutali, ndi mtendere kwa iwo apafupi;

18. kuti mwa iye ife tonse awiri tiri nao malowedwe athu kwa Atate, mwa Mzimu mmodzi.

19. Pamenepo ndipo simulinso alendo ndi ogonera, komatu muli a mudzi womwewo wa oyera mtima ndi a banja la Mulungu;

20. omangika pa maziko a atumwi ndi aneneri, pali Kristu Yesu mwini, mwala wa pangondya;

21. 1 mwa iye cimango conse, columikizika pamodzi bwino, cikula, cikhale 2 kacisi wopatulika mwa Ambuye;

22. 3 cimene inunso mumangidwamo pamodzi, mukhale cokhalamo Mulungu mwa Mzimu.

Werengani mutu wathunthu Aefeso 2