Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Yohane 1:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo cikondi ndi ici, kuti tiyende monga mwa malamulo ace. Ili ndi lamulolo, monga mudalimva kuyambira paciyambi, kuti mukayende momwemo.

7. Pakuti onyenga ambiri adaturuka kulowa m'dziko lapansi, ndiwo amene sabvomereza kuti Yesu Kristu anadza m'thupi, Ameneyo ndiye wonyenga ndi wokana Kristu.

8. Mudzipenyerere nokha, kuti mungataye zimene tazicita, koma kuti mulandire mphotho yokwanira.

9. Yense wakupitirira, wosakhala m'ciphunzitso ca Kristu, alibe Mulungu; iye wakukhala m'ciphunzitso, iyeyo ali nao Arate ndi Mwana.

Werengani mutu wathunthu 2 Yohane 1