Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Timoteo 4:15-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ameneyo iwenso ucenjere naye; pakuti anatsutsana nao mau athu.

16. Pa codzikanira canga coyamba panalibe mmodzi anandithangata, koma onse anandisiya; cimeneco cisawerengedwe cowatsutsa.

17. Koma Ambuye anaima nane nandipatsa mphamvu; kuti mwa ine cilalikiro cimveke konse konse, ndi amitundu onse amve; ndipo ndinalanditsidwa m'kamwa mwa mkango.

18. Ambuye adzandilanditsa ku nchito yonse yoipa, nadzandipulumutsa ine kulowa Ufumu wace wa Kumwamba; kwa iye ukhale ulemerero ku nthawi za nthawi. Amen.

19. Lankhula Priska ndi Akula, ndi banja la Onesiforo.

Werengani mutu wathunthu 2 Timoteo 4