Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Timoteo 3:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. ophunzira nthawi zonse, koma sakhoza konse kufikira ku cizindikiritso ca coonadi.

8. Ndipo monga momwe Yane ndi Yambre anatsutsana naye Mose, kotero iwonso atsutsana naco coonadi; ndiwo anthu obvunditsitsa mtima, osatsimikizidwa pacikhulupiriro.

9. Koma sadzapitirirapo; pakuti kupusa kwao kudzaonekeratu kwa onse, monganso kupusa kwa iwo aja.

10. Koma iwe watsatatsata ciphunzitso canga, mayendedwe, citsimikizo mtima, cikhulupiriro, kuleza mtima, cikondi, cipiriro,

11. mazunzo, kumva zowawa; zotere zonga anandicitira m'Antiokeya, m'Ikoniya, m'Lustro, mazunzo otere onga ndawamva; ndipo m'zonsezi Ambuye anandilanditsa.

12. Ndipo onse akufuna kukhala opembedza m'moyo mwa Kristu Yesu, adzamva mazunzo.

Werengani mutu wathunthu 2 Timoteo 3