Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Timoteo 2:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Uwakumbutse izi, ndi kuwacitira umboni pamaso pa Ambuye, kuti asacite makani ndi mau osapindulitsa kanthu, koma ogwetsa iwo akumva.

15. Ucite cangu kudzionetsera kwa Mulungu wobvomerezeka, wanchito wopanda cifukwa ca kucita manyazi, wolunjika nao bwino mau a coonadi.

16. Koma pewa nkhani zopanda pace; pakuti adzapitirira kutsata cisapembedzo,

17. ndipo mau ao adzanyeka cironda; a iwo ali Humenayo ndi Fileto;

18. ndiwo amene adasokera kunena za coonadi, ponena kuti kuuka kwa akufa kwacitika kale, napasula cikhulupiriro ca ena.

19. Koma ndithu maziko a Mulungu aimika pokhazikika, ndi cukhala naco cizindikilo ici, Ambuye azindikira iwo amene ali ace; ndipo, Adzipatule kwa cosalungama yense wakuehula dzina la Ambuye.

Werengani mutu wathunthu 2 Timoteo 2