Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Petro 1:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Momwemo abale, onjezani kucita cangu kukhazikitsa maitanidwe ndi masankhulidwe anu; pakuti mukacita izi, simudzakhumudwa nthawi zonse;

11. pakuti kotero kudzaonjezedwa kwa inu kolemerera khomo lakulowa ufumu wosatha wa Ambuye wathu ndi Mpulumutsi Yesu Kristu.

12. Mwa ici sindidzaleka kukukumbutsani inu nthawi zonse za izi, mungakhale muzidziwa nimukhazikika m'coonadi ciri ndi inu.

13. Ndipo ndiciyesa cokoma, pokhala ine m'msasa uwu, kukutsitsimutsani ndi kukukumbutsani;

14. podziwa kuti kuleka kwa msasa wanga kuli pafupi, monganso Ambuye wathu Yesu Kristu anandilangiza.

15. Koma ndidzacitanso cangu kosalekeza kuti nditacoka ine, mudzakhoza kukumbukila izi,

16. Pakuti sitinatsata miyambi yacabe, pamene tinakudziwitsani mphamvu ndi maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Kristu, koma tinapenya m'maso ukulu wace.

Werengani mutu wathunthu 2 Petro 1