Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 9:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakutitu za utumiki wa kwa oyera mtima sikufunika kwa ine kulembera inu;

2. pakuti ndidziwa cibvomerezo canu cimene ndidzitamandira naco cifukwa ca inu ndi Amakedoniya, kuti Akaya anakonzekeratu citapita caka; ndi cangu canu cinautsa ocurukawo.

3. Koma ndatuma abale kuti kudzitamandira kwathu kwa pa inu kusakhale kopanda pace m'menemo; kuti, monga ndinanena, mukakhale okonzekeratu;

4. kuti kapena akandiperekeze a ku Makedoniya nadzakupezani inu osakonzeka, ife (kuti tisanene inu) tingacititsidwe manyazi m'kulimbika kumene.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 9