Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 6:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani, tiri ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;

10. monga akumva cisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, lroma akulemeretsa ambiri; mensa okhala opanda-kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.

11. M'kamwa mwathu mmotseguka kwa inu Akorinto, mtima wathu wakulitsidwa.

12. Simupsinjika mwa ife, koma mupsiniika mumtima mwanu.

13. Ndipo kukhale cibwezero comweci (ndinena monga ndi ana anga) mukulitsidwe inunso.

14. Musakhale omangidwa m'goli ndi osakhulupira osiyana; pakuti cilungamo cigawanabwanji ndi cosalungama? Kapena kuunika kuyanjana bwanji nw mdima?

15. Ndipo Kristu abvomerezana bwanji ndi Beliyali? Kapena wokhulupira ali nalo gawo lanji pamodzi ndi wosakhulupira?

16. Ndipo ciphatikizo cace ncanji ndi kacisi wa Mulungu ndi wa mafano? Pakuti ife ndife kacisi wa, Mulungu wamoyo; monga Mulungu anati, Ndidzakhalitsa mwa iwo, ndipe ndidzayendayenda mwa iwo; ndipo ndidzakhala Mulungu wao, ndi iwo adzakhala anthu anga.

17. Cifukwa cace,Turukani pakati Pao, ndipo patukani, ati Ambuye,Ndipo musakhudza kanthu kosakonzeka;Ndipo Ine ndidzalandira inu,

18. Ndipo ndidzakhala kwa inu Atate,Ndi inu mudzakhala kwa Ine ana amunandi akazi,anena Ambuye Wamphamvuyonse.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 6