Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 5:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti tidziwa kuti ngati nyumba ya pansi pano ya msasa wathu ipasuka, tiri naco cimango ca kwa Mulungu, ndiyo nyumba yosamangidwa ndi manja, yosatha, m'Mwamba.

2. Pakutinso m'menemo tibuula, ndi kukhumbitsa kubvekedwa ndi cokhalamo cathu cocokera Kumwamba;

3. ngatitu pobvekedwa sitidzapezedwa amarisece.

4. Pakutinso ife okhala mu msasawu tibuula, pothodwa; si kunena kuti tifuna kubvulidwa, koma kubvekedwa, kuti caimfaco cimezedwe ndi moyo.

5. Ndipo wotikonzera ife ici cimene, ndiye Mulungu, amene anatipatsa ife cikhole ca Mzimu,

6. Pokhala nako kulimbika mtima nthawi zonse tsono, ndipo podziwa kuti pamene tiri kwathu m'thupi, sitiri kwa Ambuye,

7. (pakuti tiyendayenda mwa cikhulupiriro si mwa cionekedwe);

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 5