Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 5:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti tidziwa kuti ngati nyumba ya pansi pano ya msasa wathu ipasuka, tiri naco cimango ca kwa Mulungu, ndiyo nyumba yosamangidwa ndi manja, yosatha, m'Mwamba.

2. Pakutinso m'menemo tibuula, ndi kukhumbitsa kubvekedwa ndi cokhalamo cathu cocokera Kumwamba;

3. ngatitu pobvekedwa sitidzapezedwa amarisece.

4. Pakutinso ife okhala mu msasawu tibuula, pothodwa; si kunena kuti tifuna kubvulidwa, koma kubvekedwa, kuti caimfaco cimezedwe ndi moyo.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 5