3. popeza mwaonetsedwa kuti muli kalata wa Kristu, wakumtumikira ndi ife, wosalembedwa ndi kapezi iai, koma ndi Mzimu wa Mulungu wamoyo; wosatim'magome amiyala, koma m'magome a mitima yathupi.
4. Ndipo kulimbika kotere kwa Mulungu tiri nako mwa Kristu:
5. si kuti tiri okwanira pa ife tokha, kuyesera kanthu monga mocokera mwa ife tokha; kukwanira kwathu kucokera kwa Mulungu;
6. amenenso anatikwaniritsa ife tikhale atumiki a pangano latsopano; si la cilembo, koma la mzimu; pakuti cilembo cipha, koma mzimu ucititsa moyo.
7. Komangati utumiki wa imfa wolembedwa ndi wolocedwa m'miyala, unakhala m'ulemerero, kotero kuti ana a Israyeli sanathe kuyang'anitsa pankhope yace ya Mose, cifukwa ca ulemerero wa nkhope yace, umene unalikucotsedwa: