Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 10:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma ine ndekha Paulo, ndidandaulira inu mwa kufatsa ndi ulere wa Kristu, ine amene pamaso panu ndikhala wodzicepetsa pakati pa inu, koma pokhala kwina ine ndilimbika mtima kwa inu;

2. koma ndipempha kuti pokhala ndiri pomwepo, ndisalimbike mtima ndi kulimbika kumene ndiyesa kulimbika nako pa ena, amene atiyesera ife monga ngati tirikuyendayenda monga mwa thupi,

3. Pakuti pakuyendayenda m'thupi, siticita nkhondo monga mwa thupi,

4. (pakuti zida za nkhondo yathu siziri za thupi, koma zamphamvu mwa Mulungu zakupasula malinga);

5. ndi kugwetsa matsutsano, ndi cokwezeka conse cimene cidzikweza pokana ddziwitso ca Mulungu, ndi kugonjetsa ganizo lonse ku kumvera kwa Kristu;

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 10