Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Akorinto 1:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti monga masautso a Kristu aticurukira ife, coteronso citonthozo cathu cicuruka mwa Kristu,

6. Koma ngati tisautsidwa, kuli cifukwa ca citonthozo ndi cipulumutso canu; ngati titonthozedwa, kuli kwa citonthozo canu cimene cicititsa mwa kupirira kwa masautso omwewo amene ifenso timva.

7. Ndipo ciyembekezo cathu ca kwa inu ncokbazikika; podziwa kuti monga muli oyanjana ndi masautsowo, koteronso ndi citonthozo.

8. Pakuti sitifuna abale, kuti mukhale osadziwa za cisautso cathu tinakomana naco m'Asiya, kuti tinathodwa kwakukuru, koposa mphamvu yathu, kotero kuti tinada nkhawa ngakhale za moyo wathu;

9. koma tokha tinakhala naco citsutso ca imfa mwa ife tokha, kuti tisalimbike pa ife tokha, koma pa Mulungu wakuukitsa akufa;

10. amene anatilanditsa mu imfa yaikuru yotere, nadzalanditsa;

11. amene timyembekezera kuti adzalanditsanso; pothandizana inunso ndi pemphero lanu la kwa ife; kuti pa mphatso ya kwa ife yodzera kwa anthu ambiri, payamikike ndi anthu ambiri cifukwa ca ife.

Werengani mutu wathunthu 2 Akorinto 1