Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Yohane 5:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Wina akaona mbale wace alikucimwa cimo losati la kuimfa, apemphere Mulungu, ndipo iye adzampatsira moyo wa iwo akucita macimo osati a kuimfa. Pali cimo la kuimfa: za ililo sindinena kuti mupemphere.

17. Cosalungama ciri conse ciri ucimo; ndipo pali cimo losati la kuimfa.

18. Tidziwa kuti yense wobadwa kucokera mwa Mulungu sacimwa, koma iye wobadwa kucokera mwa Mulungu adzisunga yekha, ndipo woipayo samkhudza.

19. Tidziwa kuti tiri ife ocokera mwa Mulungu, ndipo dziko lonse lapansi ligona mwa woipayo.

20. Ndipo tidziwa kuti Mwana wa Mulungu wafika, natipatsa ife cidziwitso, kuti tizindikire Woonayo, ndipo tiri mwa Woonayo, mwa Mwana wace Yesu Kristu. Iye ndiye Mulungu woona ndi moyo wosatha.

21. Tiana, 1 dzisungireni nokha kupewa mafano.

Werengani mutu wathunthu 1 Yohane 5