Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Yohane 2:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. iye amene anena kuti ali m'kuunika, namuda mbale wace, ali mumdima kufikira tsopane lino.

10. Iye amene akonda mbale wace akhala m'kuunika, ndipo mwa iye mulibe cokhumudwitsa.

11. Koma iye wakumuda mbale wace ali mumdima, nayenda mumdima, ndipo sadziwa kumene amukako, pakuti mdima wamdetsa maso ace.

12. Ndikulemberani, tiana, popeza macimo adakhululukidwa kwa inu mwa dzina lace.

13. Ndikulemberani, atate, popeza mwamzindikira iye amene ali kuyambir paciyambi. Ndikulemberani anyamata, popeza mwamlaka woipavo, Ndakulemberani, ana, popeza mwazindikira Atate.

14. Ndakulemberani, atate, popeza mwamzindikira iye amene ali kuyambira paciyambi. Ndakulemberani, anyamata, popeza muti amphamvu, ndi mau a Mulungu akhala mwa inu, ndipo mwamlaka woipayo.

15. Musakonde dziko lapansi, kapena za m'dziko apansi. Ngati wina akonda dziko lapansi, cikondi ca Atate lsiciri mwa iye.

Werengani mutu wathunthu 1 Yohane 2