Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Yohane 2:21-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Sindinakulemberam cifukwa simudziwa coonadi, koma cifukwa muddziwa, ndi cifukwa kulibe bodza locokera kwa coonadi.

22. 4 Wabodza ndani, koma iye wokanayo kuti Yesu siali Kristu? iye ndiye wokana Kristu, amene akana Atate ndi Mwana.

23. 5 Yense wakukana Mwana, alibe Atate; wobvomereza Mwana ali ndi Atatenso.

24. Koma inu, cimene munacimva kuyambira paciyambi cikhale mwa Inu, 6 Ngari cikhala mwa inu cimene mudacimva kuyambira paciyambi, inunso mudzakhalabe mwa Mwana, ndi mwa Atate.

25. Ndipo 7 ili ndi lonjezano iye anatiloniezera ife, ndiwo moyo wosatha.

26. Izi ndakulemberani za iwo akusokeretsa inu.

27. Ndipo inu, 8 kudzoza kumene munalandira kucokera kwa iye, kukhala mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma 9 monga kudzoza kwace kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa iye.

28. Ndipo tsopano, tiana, khalani mwa iye; kuti 10 akaonekere iye tikakhale nako kulimbika mtima, osacita manyazi kwa iye pa kudza kwace.

29. Ngati mudziwa kuti ali wolungama, muzindikira kuti 11 ali yensenso wakucita cilungamo abadwa kucokera mwa iye.

Werengani mutu wathunthu 1 Yohane 2