Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Yohane 1 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mau a moyo aoneka m'thupi

1. CIMENE cinaliko kuyambira paciyambi, cimene tidacimva, cimene tidaciona m'maso mwathu, cimene tidacipenyerera, ndipo manja athu adacigwira ca Mau a moyo,

2. (ndipo moyowo unaonekera, ndipo tidaona, ndipo ticita umboni, ndipo tikulalikirani moyo wosathawo, umene unali kwa Atate, nuonekera kwa ife);

3. cimene tidaciona, ndipo tidacimva, tikulatikirani inunso, kuti inunso mukayaniane pamodzi ndi ife; ndipo ciyanjano cathu cirinso ndi Atate, ndipo ndi Mwana wace Yesu Kristu;

4. ndipo izi tilemba ife, kuti cimwemwe cathu cikwaniridwe.

Mulungu ali kuunika; wosayenda m'kuunika alibe ciyanjano ndi iye

5. Ndipo uwu ndi uthenga tidaumva kwa iye, ndipo tiulalikira kwa inu, kuti Mulungu ndiye kuunika, ndipo mwa iye monse mulibe mdima.

6. Tikati kuti tiyanjana ndi Iye, ndipo tiyenda mumdima, tinama, ndipo siticita coonadi;

7. koma ngati tiyenda m'kuunika, mongalye ali m'kuunika, tiyanjana wina ndi mnzace, ndipo mwazi wa Yesu Mwana wace utisambitsa kuticotsera ucimo wonse.

Za kuulula macimo ndi kukhululukidwa

8. Tikati kuti tiribe ucimo, tidzinyenga tokha, ndipo mwa ife mulibe coonadi.

9. Ngati tibvomereza macimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama iye, kuti atikhululukire macimo athu, ndi kutisambitsa kuticotsera cosalungama ciri conse.

10. Tikanena kutisitidacimwa, timuyesa iye wonama, ndipo mau ace sakhala mwa ife.