Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Timoteo 2:9-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Momwemonso, akazi adzibveke okha ndi cobvala coyenera, ndi manyazi, ndi cidziletso; osati ndi tsitsi lace loluka, ndi golidi kapena ngale, kapena maraya a mtengo wace wapatali;

10. komatu (umo mokomera akazi akubvomereza kulemekeza Mulungu), mwa nchito zabwino.

11. Mkazi aphunzire akhale wacete m'kumvera konse.

12. Koma sindilola ine kuti mkazi aphunzitse, kapena kulamulira mwamuna; komatu akhale cete.

13. Pakuti Adamu anayamba kulengedwa, pamenepo Heva;

14. ndipo Adamu sananyengedwa, koma mkaziyo ponyengedwa analowa m'kulakwa;

15. koma adzapulumutsidwa mwa kubala mwana, ngati akhala m'cikhulupiriro ndi cikondi ndi ciyeretso pamodzi ndi cidziletso.

Werengani mutu wathunthu 1 Timoteo 2