Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Petro 2:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndipo,Mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;kwa iwo akukhumudwa ndi mau, pokhala osamvera, kumenekonso adaikidwako.

9. Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa;

10. inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandira cifundo, koma tsopano mwalandira cifundo.

11. Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zicita nkhondo pa moyo;

12. ndipo mayendedwe anu mwa amitundu akhale okoma, kuti, m'mene akamba za inu ngati ocita zoipa, akalemekeze Mulungu pakuona nchito zanu zabwino, m'tsiku la kuyang'anira.

13. Tadzigonjani kwa zoikika zonse za anthu, cifukwa ca Ambuye; ngakhale kwa mfumu, monga mutu wa onse;

14. kapena kwa akazembe, monga otumidwa ndi iye kukalanga ocira zoipa, koma kusimba ocita zabwino.

Werengani mutu wathunthu 1 Petro 2