Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Petro 2:1-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Momwemo pakutaya coipa conse, ndi cmyengo conse, ndi maonekedwe onyenga, ndi kadoka, ndi masiniiriro onse,

2. lirani monga makanda alero mkaka woyenera, wopanda cinyengo, kuti mukakule nao kufikira cipulumutso;

3. ngati mwalawa kuti Ambuye ali wokoma mtima;

4. amene pakudza kwa iye, mwala wamoyo, wokanidwatu ndi anthu, koma ndi Mulungu wosankhika, waulemu,

5. inunso ngati miyala yamoyo mumangidwa nyumba ya uzimu, kun mukhale ansembe oyera mtima, akupereka nsembe zauzimu, zolandiridwa ndi Mulungu mwa Yesu Kristu,

6. Cifukwa kwalembedwa m'lembo,Taona, ndiika m'Ziyoni mwala wotsiriza wa pangondya, wosankhika, wa mtengo wace;Ndipo wokhulupirira iye sadzanyazitsidwa.

7. Kwa inu tsono akukhulupira, ali wa mtengo wace; koma kwa iwo osakhulupira,Mwala umene omangawo anaukana,Womwewo unayesedwa mutu wa pangondya;

8. ndipo,Mwala wakukhumudwa nao, ndi thanthwe lopunthwitsa;kwa iwo akukhumudwa ndi mau, pokhala osamvera, kumenekonso adaikidwako.

9. Koma inu ndinu mbadwa yosankhika, ansembe acifumu, mtundu woyera mtima, anthu a mw ni wace, kotero kuti mukalakire zoposazo za iye amene anakuitanani muturuke mumdima, mulowe kuunika kwace kodabwitsa;

10. inu amene kale simunali anthu, koma tsopano muli anthu a Mulungu; amene kale simunalandira cifundo, koma tsopano mwalandira cifundo.

11. Okondedwa, ndikudandaulirani ngati alendo ndi ogonera mudzikanize zilakolako za thupi zimene zicita nkhondo pa moyo;

12. ndipo mayendedwe anu mwa amitundu akhale okoma, kuti, m'mene akamba za inu ngati ocita zoipa, akalemekeze Mulungu pakuona nchito zanu zabwino, m'tsiku la kuyang'anira.

Werengani mutu wathunthu 1 Petro 2