Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Petro 1:11-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. ndi kusanthula nthawi yiti, kapena nthawi yanji Mzimu wa Kristu wokhala mwa iwo analozera, pakucitiratu umboni wa masautso a Kristu, ndi ulemerero, worsarana nao.

12. Kwa iwo amene kudabvumbulutsidwa, kuti sanadzitumikira iwo okha, koma inu, ndi zinthu izi, zimene zauzidwa kwa inu tsopano, mwa iwo amene anakulalikirani Uthenga Wabwino mwa Mzimu Woyera, wotumidwa kucokera Kumwamba; zinthu izi angelo alakalaka kusuzumiramo.

13. Mwa ici, podzimanga m'cuuno, kunena za mtima wanu, mukhale odzisunga, nimuyembekeze konse konse cisomo cirikutengedwa kudza naco kwa inu m'bvumbulutso la Yesu Kristu;

14. monga ana omvera osadzifanizitsanso ndi zilakolako zakale, pokhala osadziwa inu;

15. komatu monga iye wakuitana inu ali woyera mtima, khaiani inunso oyera mtima m'makhalidwe anu onse;

16. popeza kwalembedwa, Muzikhala oyera mtima, pakuti Ine ndine woyera mtima.

17. Ndipo mukamuitana ngati Alate, iye amene aweruza monga mwa nchito ya yense, wopanda tsankhu, khalani ndi mantha nthawi ya cilendo canu;

18. podziwa kuti simunaomboledwa ndi zobvunda, golidi ndi siliva, kusiyana nao makhalidwe anu acabe ocokera kwa makolo anu:

19. koma 1 ndi mwazi wa mtengo wace wapatali 2 monga wa mwana wa nkhosa wopanda cirema, ndi wopanda banga, ndiwo mwazi wa Kristu:

20. 3 amene anazindikirikatu lisanakhazikike dziko lapansi, koma anaonetsedwa pa citsiriziro ca nthawi,

21. cifukwa ca inu amene mwa rye mukhulupirira Mulungu 4 wakwnuukitsa iye kwa akufa, ndi kumpatsa iye ulemerero; kotero kuti cikhulupiriro canu ndi ciyembekezo canu cikhale pa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu 1 Petro 1