Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Atesalonika 5:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma za nthawizo ndi nyengozo, abale, sikufunika kuti tidzakulemberani,

2. Pakuti inu nokha mudziwa bwino kuti tsiku la Ambuye lidzadza monga mbala usiku,

3. Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo cionongeko cobukapo cidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.

4. Kama inu, abale, simuli mumdima, kuti tsikulo likakugwereni monga mbala;

5. pakuti inu nonse muli ana a kuunika, ndi ana a usana; sitiri a usiku, kapena a mdima;

6. cifukwa cace tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere,

7. Pakuti iwo akugona agona usiku; ndi iwo akuledzera aledzera usiku.

8. Koma ife popeza tiri a usana tisaledzere, titabvala capacifuwa ca cikhulupiriro ndi cikondi; ndi cisoti ciri ciyembekezo ca cipulumutso.

9. Pakuti Mulungu sanatiika ife tilawe mkwiyo, komatu kuti tilandire cipulumutso mwa Ambuye wathu Yesu Kristu,

10. amene anafa m'malo mwathu, kuti, tingakhale tidikira, tingakhale tigona, tikakhale ndi moyo pamodzi ndi Iye.

11. Mwa ici cenjezanani, ndipo mangiriranani wina ndi mnzace, monganso mumacita,

Werengani mutu wathunthu 1 Atesalonika 5