Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 9:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma ine sindinacita nako kanthu kaizi; ndipo sindilemba izi kuti cikakhale cotero ndi ine; pakuti kundikomera ine kufa, koma wina asayese kwacabe kudzitamanda kwanga.

16. Pakuti ngati ndilalikira Uthenga Wabwino ndiribe kanthu kakudzitamandira; pakuti condikakamiza ndigwidwa naco; pakuti tsoka ine ngati sindilalikira U thenga Wabwino.

17. Pakuti ngati ndicita ici cibvomerere, mphotho ndiri nayo; koma ngati si cibvomerere; anandikhulupirira m'udindo.

18. Mphotho yanga nciani tsono? Kuti pakulalikira Uthenga Wabwino ndiyese Uthenga Wabwino ukhale waulere, kuti ndisaipse ulamuliro wanga wa mu Uthenga Wabwino.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 9