20. Yense akhale m'maitanidwe m'mene anaitanidwamo.
21. Kodi unaitanidwa uli kapolo? Usasamalako; koma ngati ukhozanso kukhala mfulu, cita nako ndiko.
22. Pakuti iye amene anaitanidwa mwa Ambuye, pokhala ali kapolo, ali mfulu ya Ambuye: momwemonso woitanidwayo, pokhala ali mfulu, ali kapolo wa Kristu.
23. Munagulidwa ndi mtengo wace; musakhale akapolo a anthu.