Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 7:18-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Kodi waitanidwa wina wodulidwa? Asakhale wosadulidwa. Kodi waitanidwa wina wosadulidwa? Asadulidwe.

19. Mdulidwe ulibe kanthu, ndi kusadulidwa kulibe kanthu, koma kusunga kwa malamulo a Mulungu.

20. Yense akhale m'maitanidwe m'mene anaitanidwamo.

21. Kodi unaitanidwa uli kapolo? Usasamalako; koma ngati ukhozanso kukhala mfulu, cita nako ndiko.

22. Pakuti iye amene anaitanidwa mwa Ambuye, pokhala ali kapolo, ali mfulu ya Ambuye: momwemonso woitanidwayo, pokhala ali mfulu, ali kapolo wa Kristu.

23. Munagulidwa ndi mtengo wace; musakhale akapolo a anthu.

24. Yense, m'mene anaitanidwamo, abate, akhale momwemo ndi Mulungu.

25. Koma kunena za anamwali, ndiribe lamulo la Ambuye; koma ndikuuzani coyesa ine, monga wolandira cifundo kwa Ambuye kukhala wokhulupirika.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 7