Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Akorinto 7:15-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma ngati wosakhulupirayo acoka, acoke. M'mirandu yotere samangidwa ukapolo mbaleyo, kapena mlongoyo, Koma Mulungu watiitana ife mumtendere.

16. Pakuti udziwa bwanji mkazi iwe, ngati udzapulumutsa mwamunayo? kapena udziwa bwanji, mwamuna iwe, ngati udzapulumutsa mkazi?

17. Koma, monga Ambuye wagawira kwa yense, monga Mulungu waitana yense, momwemo ayende. Ndipo kotero ndiika m'Mipingo yonse.

18. Kodi waitanidwa wina wodulidwa? Asakhale wosadulidwa. Kodi waitanidwa wina wosadulidwa? Asadulidwe.

19. Mdulidwe ulibe kanthu, ndi kusadulidwa kulibe kanthu, koma kusunga kwa malamulo a Mulungu.

20. Yense akhale m'maitanidwe m'mene anaitanidwamo.

21. Kodi unaitanidwa uli kapolo? Usasamalako; koma ngati ukhozanso kukhala mfulu, cita nako ndiko.

22. Pakuti iye amene anaitanidwa mwa Ambuye, pokhala ali kapolo, ali mfulu ya Ambuye: momwemonso woitanidwayo, pokhala ali mfulu, ali kapolo wa Kristu.

23. Munagulidwa ndi mtengo wace; musakhale akapolo a anthu.

24. Yense, m'mene anaitanidwamo, abate, akhale momwemo ndi Mulungu.

25. Koma kunena za anamwali, ndiribe lamulo la Ambuye; koma ndikuuzani coyesa ine, monga wolandira cifundo kwa Ambuye kukhala wokhulupirika.

26. Cifukwa cace ndiyesa kuti ici ndi cokoma cifukwa ca cibvuto ca nyengo yino, kuti nkwabwino kwa munthu kukhala monga ali.

27. Kodi wamangika kwa mkazi? Usafune kumasuka. Kodi wamasuka kwa mkazi? Usafune mkazi.

28. Koma ungakhale ukwatira, sunacimwa; ndipo ngati namwali akwatiwa, sanacimwa. Koma otere adzakhala naco cisautso m'thupi, ndipo ndikulekani.

Werengani mutu wathunthu 1 Akorinto 7